< Zachariasza 8 >

1 Potem stało się słowo Pana zastępów, mówiąc:
Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
2 Tak mówi Pan zastępów: Zapaliłem się nad Syonem gorliwością wielką, owszem, rozgniewaniem wielkiem zapaliłem się.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
3 Tak mówi Pan: Nawróciłem się do Syonu, i mieszkam w pośród Jeruzalemu, aby Jeruzalem zwano miastem wiernem, a górę Pana zastępów, górą świętobliwości.
Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
4 Tak mówi Pan zastępów: Jeszcze siadać będą starcy i baby na ulicach Jeruzalemskich, mając każdy z nich laskę w ręce swej dla zeszłości wieku.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
5 Ulice także miasta pełne będą chłopiąt i dziewcząt grających na ulicach jego.
Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
6 Tak mówi Pan zastępów: Izali, że się to niepodobna widzi przed oczyma ostatków ludu tego tych dni, będzie też to niepodobna przed oczyma mojemi? mówi Pan zastępów.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 Tak mówi Pan zastępów: Oto Ja wybawię lud mój z ziemi na wschód, i z ziemi na zachód słońca.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
8 I przywiodę ich zaś; a będą mieszkać w pośród Jeruzalemu, i będą ludem moim, a Ja będę Bogiem ich w prawdzie i w sprawiedliwości.
Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
9 Tak mówi Pan zastępów: Niech się zmocnią ręce wasze, którzyście słuchali w tych dniach słów tych z ust proroków, którzy byli ode dnia, którego założony jest dom Pana zastępów, że kościół ma być dobudowany.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
10 Bo się przed temi dniami praca ludzka i praca bydląt nie nagradzała, nawet wychodzącemu i wchodzącemu nie było pokoju dla nieprzyjaciela; bom Ja spuścił wszystkich ludzi jednego z drugim.
Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
11 Lecz teraz nie tak jako za dni przeszłych czynię ostatkowi ludu tego, mówi Pan zastępów:
Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 Ale siewy macie spokojne; winna macica wydaje owoc swój, i ziemia wydaje urodzaj swój, niebiosa także wydawają rosę twoję, a to wszystko daję w osiadłość ostatkom ludu tego.
“Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
13 I stanie się, że jakoście byli przeklęstwem między poganami, o domie Judzki i domie Izraelski! tak was zaś będę ochraniał, i będziecie błogosławieństwem; nie bójcie się, niech się zmacniają ręce wasze.
Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
14 Bo tak mówi Pan zastępów: Jakom wam był umyślił źle uczynić, gdy mię do gniewu pobudzali ojcowie wasi, mówi Pan zastępów, a nie żałowałem tego,
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
15 Tak nawróciwszy się umyśliłem w te dni dobrze czynić Jeruzalemowi i domowi Judzkiemu; nie bójcież się.
“Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
16 Teć są rzeczy, które czynić będziecie: Prawdę mówcie każdy z bliźnim swoim, prawy i spokojny sąd czyńcie w bramach waszych;
Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
17 A jeden drugiemu nic złego nie myślcie w sercach waszych, a w krzywoprzysięstwie się nie kochajcie; bo to wszystko jest, czego nienawidzę, mówi Pan.
musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
18 I stało się słowo Pana zastępów do mnie, mówiąc:
Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
19 Tak mówi Pan zastępów: Post czwartego, i post piątego, i post siódmego, i post dziesiątego miesiąca obróci się domowi Judzkiemu w radość i wesele, i w rozkoszne uroczyste święta; ale prawdę i pokój miłujcie.
Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
20 Tak mówi Pan zastępów: Jeszczeć będą przychodzić narody i obywatele wielu miast;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
21 Przychodzić, mówię, będą obywatele jednego miasta do drugiego, mówiąc: Pójdźmy ochotnie błagać oblicze Pańskie, a szukać Pana zastępów; i rzecze każdy: Pójdę i ja.
ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
22 A tak wiele ludu i narodów niezliczonych przyjdzie szukać Pana zastępów w Jeruzalemie, i błagać oblicze Pańskie.
Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
23 Tak mówi Pan zastępów: W one dni uchwycą się dziesięć mężów ze wszystkich języków onych narodów; uchwycą się, mówię, podołka jednego Żyda, mówiąc: Pójdziemy z wami, bo słyszymy, że Bóg jest z wami.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”

< Zachariasza 8 >