< Salmos 116 >

1 Amo o SENHOR, porque ele escuta minha voz [e] minhas súplicas.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Porque ele tem inclinado a mim seus ouvidos; por isso eu clamarei a ele em [todos] os meus dias.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Cordas da morte me cercaram, e angústias do Xeol me afrontaram; encontrei opressão e aflição. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 Mas clamei ao nome do SENHOR, [dizendo]: Ah SENHOR, livra minha alma!
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 O SENHOR é piedoso e justo; e nosso Deus é misericordioso.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 O SENHOR protege os simples; eu estava com graves problemas, mas ele me livrou.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Minha alma, volta ao teu descanso, pois o SENHOR tem te tratado bem.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Porque tu, [SENHOR], livraste minha alma da morte, meus olhos das lágrimas, e meu pé do tropeço.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Andarei diante do SENHOR na terra dos viventes.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Eu cri, por isso falei; estive muito aflito.
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Eu dizia em minha pressa: Todo homem é mentiroso.
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 O que pagarei ao SENHOR por todos os benefícios dele para mim?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Tomarei o copo da salvação, [e] chamarei o nome do SENHOR.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Certamente pagarei meus votos ao SENHOR, na presença de todo o seu povo.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Preciosa é aos olhos do SENHOR a morte de seus santos.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Ah SENHOR, verdadeiramente eu sou teu servo; sou teu servo, filho de tua serva; tu me soltaste das correntes que me prendiam.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Sacrificarei a ti sacrifício de agradecimento, e chamarei o nome do SENHOR.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Certamente pagarei meus votos ao SENHOR, na presença de todo o seu povo;
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 Nos pátios da casa do SENHOR, em meio de ti, ó Jerusalém. Aleluia!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Salmos 116 >