< Книга Екклезиаста 1 >

1 Глаголы Екклесиаста, сына Давидова, царя Израилева во Иерусалиме.
Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2 Суета суетствий, рече Екклесиаст, суета суетствий, всяческая суета.
“Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
3 Кое изюбилие человеку во всем труде его, имже трудится под солнцем?
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4 Род преходит и род приходит, а земля во век стоит.
Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5 И восходит солнце и заходит солнце и в место свое влечется, сие возсиявая тамо.
Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6 Идет к югу и обходит к северу, обходит окрест, идет дух и на круги своя обращается дух.
Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7 Вси потоцы идут в море, и море несть насыщаемо: на место, аможе потоцы идут, тамо тии возвращаются ити.
Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
8 Вся словеса трудна, не возможет муж глаголати: и не насытится око зрети, ни исполнится ухо слышания.
Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9 Что было, тожде есть, еже будет: и что было сотвореное, тожде имать сотворитися:
Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10 и ничтоже ново под солнцем. Иже возглаголет и речет: се, сие ново есть: уже бысть в вецех бывших прежде нас.
Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
11 Несть память первых, и последним бывшым не будет их память с будущими на последок.
Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
12 Аз Екклесиаст бых царь над Израилем во Иерусалиме
Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
13 и вдах сердце мое, еже взыскати и разсмотрити в мудрости о всех бывающих под небесем: яко попечение лукаво даде Бог сыном человеческим, еже упражднятися в нем.
Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
14 Видех всяческая сотворения сотворенная под солнцем: и се, вся суетство и произволение духа.
Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15 Развращенное не может исправитися, и лишение не может изчислитися.
Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16 Глаголах аз в сердцы моем, еже рещи: се, аз возвеличихся и умножих мудрость паче всех, иже быша прежде мене во Иерусалиме,
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
17 и сердце мое вдах, еже ведети премудрость и разум: и сердце мое виде многая, премудрость и разум, притчи и хитрость: уразумех аз, яко и сие есть произволение духа:
Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18 яко во множестве мудрости множество разума, и приложивый разум приложит болезнь.
Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.

< Книга Екклезиаста 1 >