< Книга пророка Осии 3 >

1 И рече Господь ко мне: еще иди и возлюби жену любящую зло и любодейцу, якоже любит Бог сыны Израилевы: сии же взирают к богом чуждим и любят варения с коринками.
Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
2 И наях себе оную пятиюнадесять сребрениками и гомором ячменя и невелем вина,
Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
3 и рекох ей: дни многи да седиши у мене и аз у тебе, и не соблудиши, ни будеши мужу иному:
Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
4 зане дни многи сядут сынове Израилевы, не сущу царю, ни сущу князю, ни сущей жертве, ни сущу жертвеннику, ни жречеству, ниже явлением:
Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
5 и посем обратятся сынове Израилевы и взыщут Господа Бога своего и Давида царя своего, и почудятся о Господе и о благостех Его в последния дни.
Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.

< Книга пророка Осии 3 >