< Псалтирь 3 >

1 Псалом Давиду, внегда отбегаше от лица Авессалома сына своего. Господи, что ся умножиша стужающии ми? Мнози востают на мя,
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
2 мнози глаголют души моей: несть спасения ему в Бозе его.
Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
3 Ты же, Господи, заступник мой еси, слава моя, и возносяй главу мою.
Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 Гласом моим ко Господу воззвах, и услыша мя от горы святыя Своея.
Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
5 Аз уснух, и спах, востах, яко Господь заступит мя.
Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 Не убоюся от тем людий, окрест нападающих на мя.
Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 Воскресени, Господи, спаси мя, Боже мой: яко Ты поразил еси вся враждующыя ми всуе, зубы грешников сокрушил еси.
Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
8 Господне есть спасение, и на людех Твоих благословение Твое.
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)

< Псалтирь 3 >