< Proverbios 16 >

1 Del hombre son las preparaciones del corazón: mas de Jehová la respuesta de la lengua.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Todos los caminos del hombre son limpios en su opinión: mas Jehová pesa los espíritus.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Encomienda a Jehová tus obras; y tus pensamientos serán afirmados.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Todas las cosas ha hecho Jehová por sí mismo; y aun al impío para el día malo.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Abominación es a Jehová todo altivo de corazón: la mano junta a la mano, no será sin castigo.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Con misericordia y verdad será reconciliado el pecado; y con el temor de Jehová se aparta del mal.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Cuando los caminos del hombre serán agradables a Jehová, aun sus enemigos pacificará con él.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Mejor es lo poco con justicia, que la muchedumbre de los frutos sin derecho.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 El corazón del hombre piensa su camino: mas Jehová endereza sus pasos.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Adivinación está en los labios del rey: en juicio no prevaricará su boca.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Peso y balanzas derechas son de Jehová: obra suya son todas las pesas de la bolsa.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Abominación es a los reyes hacer impiedad; porque con justicia será confirmado su trono.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Los labios justos son el contentamiento de los reyes; y al que habla lo recto aman.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 La ira del rey es mensajero de muerte: mas el hombre sabio la evitará.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 En la alegría del rostro del rey está la vida; y su benevolencia es como la nube tardía.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Mejor es adquirir sabiduría que oro preciado; y adquirir inteligencia vale más que la plata.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 El camino de los rectos es apartarse del mal: su alma guarda, el que guarda su camino.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Antes del quebrantamiento es la soberbia; y antes de la caída, la altivez de espíritu.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Mejor es abajar el espíritu con los humildes, que partir despojos con los soberbios.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 El entendido en la palabra, hallará el bien; y el que confía en Jehová, bienaventurado él.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 El sabio de entendimiento es llamado entendido; y la dulzura de labios aumentará la doctrina.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Manadero de vida es el entendimiento al que le posee: mas la erudición de los insensatos es locura.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 El corazón del sabio hace prudente su boca; y con sus labios aumenta la doctrina.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Panal de miel son las hablas suaves, suavidad al alma, y medicina a los huesos.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 Hay camino que es derecho al parecer del hombre: mas su salida son caminos de muerte.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 El alma del que trabaja, trabaja para sí; porque su boca le constriñe.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 El hombre perverso cava en busca del mal; y en sus labios es como llama de fuego.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 El hombre perverso levanta contienda; y el chismoso aparta los príncipes.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 El hombre malo lisonjea a su prójimo; y le hace caminar por el camino no bueno:
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Cierra sus ojos para pensar perversidades: mueve sus labios, efectúa el mal.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Corona de honra es la vejez: en el camino de justicia se hallará.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Mejor es el que tarde se aira, que el fuerte; y el que se enseñorea de su espíritu, que el que toma una ciudad.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 La suerte se echa en el seno: mas de Jehová es todo su juicio.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Proverbios 16 >