< Proverbios 1 >

1 LOS proverbios de Salomón, hijo de David, rey de Israel:
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Para entender sabiduría y doctrina; para conocer las razones prudentes;
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 Para recibir el consejo de prudencia, justicia, y juicio y equidad;
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 Para dar sagacidad á los simples, y á los jóvenes inteligencia y cordura.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Oirá el sabio, y aumentará el saber; y el entendido adquirirá consejo;
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 Para entender parábola y declaración; palabras de sabios, y sus dichos oscuros.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 El principio de la sabiduría es el temor de Jehová: los insensatos desprecian la sabiduría y la enseñanza.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Oye, hijo mío, la doctrina de tu padre, y no desprecies la dirección de tu madre:
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Porque adorno de gracia serán á tu cabeza, y collares á tu cuello.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Hijo mío, si los pecadores te quisieren engañar, no consientas.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Si dijeren: Ven con nosotros, pongamos asechanzas á la sangre, acechemos sin motivo al inocente;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Los tragaremos vivos como el sepulcro, y enteros, como los que caen en sima; (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Hallaremos riquezas de todas suertes, henchiremos nuestras casas de despojos;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Echa tu suerte entre nosotros; tengamos todos una bolsa:
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Hijo mío, no andes en camino con ellos; aparta tu pie de sus veredas:
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Porque sus pies correrán al mal, é irán presurosos á derramar sangre.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Porque en vano se tenderá la red ante los ojos de toda ave;
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 Mas ellos á su propia sangre ponen asechanzas, y á sus almas tienden lazo.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Tales son las sendas de todo el que es dado á la codicia, [la cual] prenderá el alma de sus poseedores.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 La sabiduría clama de fuera, da su voz en las plazas:
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 Clama en los principales lugares de concurso; en las entradas de las puertas de la ciudad dice sus razones:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 ¿Hasta cuándo, oh simples, amaréis la simpleza, y los burladores desearán el burlar, y los insensatos aborrecerán la ciencia?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Volveos á mi reprensión: he aquí yo os derramaré mi espíritu, y os haré saber mis palabras.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Por cuanto llamé, y no quisisteis; extendí mi mano, y no hubo quien escuchase;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Antes desechasteis todo consejo mío, y mi reprensión no quisisteis:
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 También yo me reiré en vuestra calamidad, y me burlaré cuando [os] viniere lo que teméis;
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 Cuando viniere como una destrucción lo que teméis, y vuestra calamidad llegare como un torbellino; cuando sobre vosotros viniere tribulación y angustia.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Entonces me llamarán, y no responderé; buscarme han de mañana, y no me hallarán:
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Por cuanto aborrecieron la sabiduría, y no escogieron el temor de Jehová,
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Ni quisieron mi consejo, y menospreciaron toda reprensión mía:
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Comerán pues del fruto de su camino, y se hartarán de sus consejos.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Porque el reposo de los ignorantes los matará, y la prosperidad de los necios los echará á perder.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Mas el que me oyere, habitará confiadamente, y vivirá reposado, sin temor de mal.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Proverbios 1 >