< Job 12 >

1 Y Job respondió y dijo:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Sin duda ustedes son el pueblo, y la sabiduría terminará con ustedes.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Pero tengo una mente como ustedes; Soy igual a ustedes: sí, ¿quién no tiene conocimiento de cosas como estas?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 ¡Parece que debo ser como uno que es motivo de burla a su prójimo, uno que hace su oración a Dios y recibe respuesta! ¡El hombre recto que no ha hecho nada malo es escarnecido!
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 En el pensamiento de aquel que está a gusto, no hay respeto por alguien que está en problemas; tal es el destino de aquellos cuyos pies se están deslizando.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Hay abundancia en las tiendas de aquellos que hacen la destrucción, y aquellos por quienes Dios es movido a la ira están a salvo; incluso aquellos los que Dios les ha dado el poder.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Pero ahora pregunta a las bestias, y aprende de ellas; o a las aves del cielo, y te informarán;
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 O a las cosas en la tierra, y te darán sabiduría; Y los peces del mar te darán noticias de ello.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 ¿Quién no ve por todos estos que la mano del Señor ha hecho esto?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 En cuya mano está el alma de todo ser viviente, y el aliento de toda carne humana.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 ¿No son las palabras probadas por el oído, al igual que la comida se prueba por la boca?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Los ancianos tienen sabiduría, y una larga vida da conocimiento.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 En Dios hay sabiduría y poder. El consejo y el conocimiento son suyos.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 En verdad, no hay reconstrucción de lo que es derribado por Dios; cuando un hombre es aprisionado por Dios, nadie puede soltarlo.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 En verdad, él retiene las aguas y están secas; Él los envía y la tierra se inunda.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Con él están el poder y la sabiduría; el que es guiado al error, junto con su guía, está en sus manos;
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Él quita la sabiduría de los guías sabios, y hace que los jueces sean necios;
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Él deshace las cadenas de los reyes, y ata sus cinturas con lazos;
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Él hace a los sacerdotes prisioneros, volcando a los que están en posiciones seguras;
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Él hace las palabras de personas responsables sin efecto, y quita el entendimiento a los ancianos;
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Él avergüenza a los jefes, y quita el poder de los fuertes;
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Descubriendo cosas profundas de la oscuridad, y saca la sombra profunda a la luz;
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Engrandece a las naciones y las destruye; Extendiendo las tierras de los pueblos, y luego las reúne.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Él quita la sabiduría de los gobernantes de la tierra, y los envía vagando en un desierto donde no hay camino.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 Ellos van a tientas en la oscuridad sin luz, tambaleándose, como los borrachos.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Job 12 >