< 1 Korintliler 11 >

1 Mesih'i örnek aldığım gibi, siz de beni örnek alın.
Tsatirani chitsanzo changa, monga inenso nditsatira chitsanzo cha Khristu.
2 Her durumda beni anımsadığınız ve size ilettiğim öğretileri olduğu gibi koruduğunuz için sizi övüyorum.
Ndikukuyamikani chifukwa chondikumbukira pa zonse ndiponso posunga ziphunzitso monga ndinakuphunzitsirani.
3 Ama şunu da bilmenizi isterim: Her erkeğin başı Mesih, kadının başı erkek, Mesih'in başı da Tanrı'dır.
Tsopano ndikufuna muzindikire kuti Khristu ndiye mutu wa munthu aliyense, ndipo mwamuna ndiye mutu wamkazi, ndipo mutu wa Khristu ndi Mulungu.
4 Başına bir şey takıp dua ya da peygamberlik eden her erkek, başını küçük düşürür.
Mwamuna aliyense wopemphera kapena kunenera ataphimba mutu wake akunyoza mutu wakewo.
5 Ama başı açık dua ya da peygamberlik eden her kadın, başını küçük düşürür. Böylesinin, başı tıraş edilmiş bir kadından farkı yoktur.
Ndipo mkazi aliyense wopemphera kapena kunenera asanaphimbe mutu wake sakulemekeza mutu wakewo. Kuli chimodzimodzi kumeta mutu wake.
6 Kadın başını açarsa, saçını kestirsin. Ama kadının saçını kestirmesi ya da tıraş etmesi ayıpsa, başını örtsün.
Ngati mkazi saphimba kumutu kwake, ndiye kuti amete tsitsi lake. Ngati nʼchamanyazi kwa mkazi kungoyepula kapena kumeta mpala, ndiye kuti aphimbe kumutu kwake.
7 Erkek başını örtmemeli; o, Tanrı'nın benzeri ve yüceliğidir. Kadın da erkeğin yüceliğidir.
Mwamuna sayenera kuphimba kumutu popeza ndi chifaniziro ndi ulemerero wa Mulungu; pamene mkazi ndi ulemerero wa mwamuna.
8 Çünkü erkek kadından değil, kadın erkekten yaratıldı.
Pakuti mwamuna sachokera kwa mkazi, koma mkazi kwa mwamuna.
9 Erkek kadın için değil, kadın erkek için yaratıldı.
Ndipo mwamuna sanalengedwe chifukwa cha mkazi, koma mkazi analengedwera mwamuna.
10 Bu nedenle ve melekler uğruna kadının başı üzerinde yetkisi olmalıdır.
Pa chifukwa ichi, ndiponso pa chifukwa cha angelo, mkazi akuyenera kukhala ndi chizindikiro cha ulamuliro wake.
11 Ne var ki, Rab'de ne kadın erkekten ne de erkek kadından bağımsızdır.
Komabe mwa Ambuye, mkazi amadalira mwamuna ndipo mwamuna amadalira mkazi.
12 Çünkü kadın erkekten yaratıldığı gibi, erkek de kadından doğar. Ama her şey Tanrı'dandır.
Pakuti monga mkazi anachokera kwa mwamuna, momwemonso mwamuna anabadwa mwa mkazi. Koma zonse zichokera kwa Mulungu.
13 Siz kendiniz karar verin: Kadının açık başla Tanrı'ya dua etmesi uygun mu?
Dziweruzeni. Kodi nʼchabwino kuti mkazi apemphere kwa Mulungu wopanda chophimba kumutu?
14 Doğanın kendisi bile size erkeğin uzun saçlı olmasının kendisini küçük düşürdüğünü, kadının uzun saçlı olmasının ise kendisini yücelttiğini öğretmiyor mu? Çünkü saç kadına örtü olarak verilmiştir.
Kodi chikhalidwe chathu sichitiphunzitsa kuti nʼchamanyazi kuti mwamuna akhale ndi tsitsi lalitali,
koma mkazi akakhala ndi tsitsi lalitali ndi ulemerero wake? Pakuti mkazi anapatsidwa tsitsi lalitali monga chophimba kumutu.
16 Bu konuda çekişmek isteyen varsa, şunu bilsin ki, bizim ya da Tanrı'nın kiliselerinin böyle bir alışkanlığı yoktur.
Ngati wina akufuna kutsutsapo pa zimenezi, ife ndiponso mipingo ya Mulungu tilibe machitidwe ena apadera koma ndi omwewa.
17 Toplantılarınız yarardan çok zarar getirdiği için aşağıdaki uyarıları yaparken sizi övemem.
Koma popereka malangizo awa sindikufuna kukuyamikirani popeza mʼmisonkhano yanu mumachita zoyipa kuposa zabwino.
18 Birincisi, toplulukça bir araya geldiğinizde aranızda ayrılıklar olduğunu duyuyorum. Buna biraz da inanıyorum.
Choyamba, ndikumva kuti mukasonkhana mu mpingo mumasankhana ndipo ndikukhulupirira kuti zimenezi kwinaku nʼzoona.
19 Çünkü Tanrı'nın beğenisini kazananların belli olması için aranızda bölünmeler olması gerekiyor!
Nʼzosakayikitsa kuti pali kugawikana pakati panu kuti adziwike amene ndi ovomerezeka ndi Mulungu.
20 Toplandığınızda Rab'bin Sofrası'na katılmak için toplanmıyorsunuz.
Tsono, mukasonkhana pamodzi, chimene mumadya si Mgonero wa Ambuye.
21 Her biriniz ötekini beklemeden kendi yemeğini yiyor. Kimi aç kalıyor, kimi sarhoş oluyor.
Pakuti mukamadya, aliyense amangodzidyera zomwe anakonza. Wina amakhala ndi njala pamene wina amaledzera.
22 Yiyip içmek için evleriniz yok mu? Tanrı'nın topluluğunu hor mu görüyorsunuz, yiyeceği olmayanları utandırmak mı istiyorsunuz? Size ne diyeyim? Sizi öveyim mi? Bu konuda övemem!
Kodi mulibe nyumba zanu kumene mungamadyere ndi kumwa? Kapena mumapeputsa mpingo wa Mulungu ndi kuchititsa manyazi amene alibe kalikonse? Ndikunena chiyani kwa inu? Moti ndikuyamikireni pa zimenezi? Ayi, pa zinthu izi sindingakuyamikireni.
23 Size ilettiğimi ben Rab'den öğrendim. Ele verildiği gece Rab İsa eline ekmek aldı, şükredip ekmeği böldü ve şöyle dedi: “Bu sizin uğrunuza feda edilen bedenimdir. Beni anmak için böyle yapın.”
Pakuti zimene ndinalandira kwa Ambuye ndi zomwe ndinakupatsani. Ambuye Yesu, usiku umene anaperekedwa uja, anatenga buledi.
Atayamika ndi kumunyema ananena kuti, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”
25 Aynı biçimde yemekten sonra kâseyi alıp şöyle dedi: “Bu kâse kanımla gerçekleşen yeni antlaşmadır. Her içtiğinizde beni anmak için böyle yapın.”
Chimodzimodzi, atatha kudya, anatenga chikho, nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga; imwani nthawi zonse pokumbukira Ine.”
26 Bu ekmeği her yediğinizde ve bu kâseden her içtiğinizde, Rab'bin gelişine dek Rab'bin ölümünü ilan etmiş olursunuz.
Pakuti nthawi zonse pamene mudya bulediyu ndikumwa chikhochi, mukulalikira imfa ya Ambuye mpaka Iye adzabweranso.
27 Bu nedenle kim uygun olmayan biçimde ekmeği yer ya da Rab'bin kâsesinden içerse, Rab'bin bedenine ve kanına karşı suç işlemiş olur.
Chifukwa chake, aliyense amene adya buledi kapena kumwa chikho cha Ambuye mʼnjira yosayenera adzachimwira thupi ndi magazi a Ambuye.
28 Kişi önce kendini sınasın, sonra ekmekten yiyip kâseden içsin.
Munthu adzisanthule yekha asanadye buledi kapena kumwa chikhochi.
29 Çünkü bedeni farketmeden yiyip içen, böyle yiyip içmekle kendi kendini mahkûm eder.
Popeza aliyense amene adya kapena kumwa mosazindikira thupi la Ambuye, amadya ndi kumwa chiweruzo chake chomwe.
30 İşte bu yüzden birçoğunuz zayıf ve hastadır, bazılarınız da ölmüştür.
Nʼchifukwa chake pakati panu ambiri mwa inu ndi ofowoka ndi odwala, ndipo ambirinso agona tulo.
31 Kendimizi doğrulukla yargılasaydık, yargılanmazdık.
Koma tikanadziyesa tokha sitikaweruzidwanso.
32 Dünyayla birlikte mahkûm olmayalım diye Rab bizi yargılayıp terbiye ediyor.
Pamene tiweruzidwa ndi Ambuye, ndiye kuti akukonza khalidwe lathu kupewa kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi anthu osakhulupirira.
33 Öyleyse kardeşlerim, yemek için bir araya geldiğinizde birbirinizi bekleyin.
Ndiye tsono abale anga, pamene musonkhana pa chakudya, mudikirirane.
34 Aç olan karnını evde doyursun. Öyle ki, toplanmanız yargılanmanıza yol açmasın. Öbür sorunları ise geldiğimde çözerim.
Ngati wina ali ndi njala, adye ku nyumba kwake kuti pamene musonkhana pamodzi zisafike poti muweruzidwe nazo. Ndipo ndikabwera ndidzakupatsani malangizo ena owonjezera.

< 1 Korintliler 11 >