< 1 Korintliler 7 >

1 Şimdi bana yazdığınız konulara gelelim: “Erkeğin kadına dokunmaması iyidir” diyorsunuz.
Tsopano pa zinthu zomwe munandilembera nʼkwabwino kuti munthu asakwatire.
2 Ama fuhuştan ötürü her erkek karısıyla, her kadın da kocasıyla yaşasın.
Koma chifukwa choti chigololo chawanda, mwamuna aliyense akhale naye mkazi wakewake ndipo mkazi aliyense akhale naye mwamuna wakewake.
3 Erkek karısına, kadın da kocasına hakkını versin.
Mwamuna akwaniritse udindo wake wa pa banja kwa mkazi wake, ndipo chimodzimodzi mkazi kwa mwamuna wake.
4 Kadının bedeni kendisine değil, kocasına aittir. Bunun gibi, erkeğin bedeni de kendisine değil, karısına aittir.
Thupi la mkazi wokwatiwa si la iye mwini yekha koma ndi la mwamuna wakenso. Momwemonso, thupi la mwamuna si la iye mwini yekha koma ndi la mkazi wakenso.
5 Geçici bir süre için anlaşıp kendinizi duaya vermekten başka bir nedenle birbirinizi mahrum etmeyin. Sonra yine birleşin ki, kendinizi denetleyemediğiniz için Şeytan sizi ayartmasın.
Musamakanizane, pokhapokha mutagwirizana awiri kuti mwakanthawi mudzipereke kumapemphero. Kenaka mukhalirenso pamodzi kuopa kuti Satana angakuyeseni chifukwa cholephera kudziretsa.
6 Bunu bir buyruk olarak değil, bir uzlaşma yolu olarak söylüyorum.
Ndikunena zimenezi mokulolani chabe osati mokulamulani.
7 Herkesin benim gibi olmasını dilerdim. Ama herkesin Tanrı'dan aldığı ruhsal bir armağanı vardır; kiminin şöyle, kiminin böyle.
Ine ndikanakonda anthu akanakhala ngati ine. Koma poti munthu aliyense ali ndi mphatso yakeyake yochokera kwa Mulungu, wina mphatso yake, wina yakenso.
8 Yine de evli olmayanlarla dul kadınlara şunu söyleyeyim: Benim gibi kalsalar kendileri için iyi olur.
Tsono kwa osakwatira onse, ndi akazi amasiye ndikuti, ndi bwino kwa iwo kukhala osakwatira monga mmene ndilili inemu.
9 Ama kendilerini denetleyemiyorlarsa, evlensinler. Çünkü için için yanmaktansa evlenmek daha iyidir.
Koma ngati sangathe kudziretsa, akwatire, popeza ndi bwino kukwatira kusiyana ndi kudzizunza ndi chilakolako.
10 Evlilereyse şunu buyuruyorum, daha doğrusu Rab buyuruyor: Kadın kocasından ayrılmasın.
Kwa amene ali pa banja ndikupatsani lamulo ili (osati langa koma la Ambuye): Mkazi asalekane ndi mwamuna wake.
11 Ayrılırsa evlenmesin, ya da kocasıyla barışsın. Erkek de karısını boşamasın.
Koma ngati atatero, asakwatiwenso, apo ayi, abwerere kwa mwamuna wakeyo. Ndipo mwamuna asaleke mkazi wake.
12 Geri kalanlara Rab değil, ben söylüyorum: Eğer bir kardeşin karısı iman etmemişse ama kendisiyle yaşamaya razıysa, onu boşamasın.
Kwa ena onse ndikunena izi (ineyo osati Ambuye); ngati mʼbale wina ali ndi mkazi wosakhulupirira ndipo mkaziyo walola kukhala pa banja ndi mʼbaleyo, ameneyo asamuleke.
13 Bir kadının kocası iman etmemişse ama kendisiyle yaşamaya razıysa, kadın onu boşamasın.
Ngati mayi wina ali ndi mwamuna wosakhulupirira ndipo mwamunayo walola kukhala pa banja ndi mayiyo, ameneyo asamuleke.
14 Çünkü iman etmemiş koca karısı aracılığıyla, iman etmemiş kadın da imanlı kocası aracılığıyla kutsanır. Yoksa çocuklarınız murdar olurdu. Ama şimdi kutsaldırlar.
Pakuti mwamuna wosakhulupirirayo amayeretsedwa chifukwa cha mkazi wakeyo, ndipo mkazi wosakhulupirira amayeretsedwa chifukwa cha mwamuna wokhulupirirayo. Kupanda apo ana anu akanakhala odetsedwa, koma mmene zililimu ndi oyeretsedwa.
15 İman etmeyen ayrılırsa ayrılsın. Kardeş ya da kızkardeş böyle durumlarda özgürdür. Tanrı sizi barış içinde yaşamaya çağırdı.
Koma ngati wosakhulupirira achoka, mulekeni achoke. Zikatero ndiye kuti mwamuna kapena mkazi wokhulupirirayo sali womangikanso. Mulungu anatiyitana kuti tikhale mu mtendere.
16 Ey kadın, kocanı kurtarıp kurtaramayacağını nereden biliyorsun? Ey erkek, karını kurtarıp kurtaramayacağını nereden biliyorsun?
Kodi iwe, mkazi, ungadziwe bwanji kuti mwina nʼkupulumutsa mwamuna wako? Kapena iwe, mwamuna, ungadziwe bwanji kuti mwina nʼkupulumutsa mkazi wako?
17 Ancak herkes Rab'bin kendisi için belirlediği duruma uygun biçimde, Tanrı'dan aldığı çağrıya göre yaşasın. Bunu bütün kiliselere buyuruyorum.
Koma aliyense akhale moyo umene Ambuye anamupatsa, umene Mulungu anamuyitanira. Ili ndiye lamulo limene ndalikhazikitsa mʼmipingo yonse.
18 Biri sünnetliyken mi çağrıldı, sünnetsiz olmasın. Bir başkası sünnetsizken mi çağrıldı, sünnet olmasın.
Ngati pamene munthu amayitanidwa anali atachita mdulidwe, asavutike nʼkubisa za mdulidwe wakewo. Ngatinso pamene munthu amayitanidwa nʼkuti asanachite mdulidwe, asachite mdulidwe.
19 Sünnetli olup olmamak önemli değildir. Önemli olan, Tanrı'nın buyruklarını yerine getirmektir.
Mdulidwe si kanthu, kusachita mdulidwe si kanthunso. Chofunika nʼkusunga malamulo a Mulungu.
20 Herkes ne durumda çağrıldıysa, o durumda kalsın.
Aliyense akhale monga analili pamene Mulungu anamuyitana.
21 Köleyken mi çağrıldın, üzülme. Ama özgür olabilirsen, fırsatı kaçırma!
Kodi munali kapolo pamene Mulungu anakuyitanani? Musavutike nazo zimenezi. Koma ngati mutapeza mwayi woti mulandire ufulu, ugwiritseni ntchito mwayiwo.
22 Çünkü Rab'bin çağrısını aldığı zaman köle olan kimse, şimdi Rab'bin özgürüdür. Özgürken çağrılan kişi de Mesih'in kölesidir.
Pakuti amene anali kapolo pamene amayitanidwa ndi Ambuye, ndi mfulu wa Ambuye; chimodzimodzinso amene anali mfulu pamene anayitanidwa, ndi kapolo wa Khristu.
23 Bir bedel karşılığı satın alındınız, insanlara köle olmayın.
Munagulidwa ndi mtengowapatali, choncho musakhalenso akapolo a anthu.
24 Kardeşler, herkes ne durumda çağrıldıysa, Tanrı önünde o durumda kalsın.
Abale, aliyense angokhala pamaso pa Mulungu monga momwe analili pamene Mulungu anamuyitana.
25 Kızlara gelince, Rab'den onlarla ilgili bir buyruk almış değilim. Ama Rab'bin merhameti sayesinde güvenilir biri olarak düşündüklerimi söylüyorum.
Tsopano za anamwali: Ine ndilibe lamulo lochokera kwa Ambuye, koma ndipereka maganizo anga monga ngati munthu amene mwachifundo cha Ambuye ndine wodalirika.
26 Öyle sanıyorum ki, şimdiki sıkıntılar nedeniyle insanın olduğu gibi kalması iyidir.
Chifukwa cha masautso a masiku ano, ndikuganiza kuti nʼkwabwino kuti munthu akhale monga mmene alili.
27 Karın varsa, boşanmayı isteme. Karın yoksa, kendine eş arama.
Kodi ndinu wokwatira? Musalekane. Kodi ndinu wosakwatira? Musafunefune mkazi.
28 Ama evlenirsen günah işlemiş olmazsın. Bir kız da evlenirse günah işlemiş olmaz. Ne var ki, evlenenler bu yaşamda sıkıntılarla karşılaşacak. Ben sizi bu sıkıntılardan esirgemek istiyorum.
Komabe ngati mukwatira simunachimwe; ndipo ngati namwali akwatiwa sanachimwenso. Koma amene walowa mʼbanja adzakumana ndi zovuta zambiri mʼmoyo uno, ndipo sindikufuna kuti inu mukumane ndi zovutazi.
29 Kardeşler, şunu demek istiyorum: Zaman daralmıştır. Bundan böyle, karısı olanlar karıları yokmuş gibi, yas tutanlar yas tutmuyormuş gibi, sevinenler sevinmiyormuş gibi, mal alanlar malları yokmuş gibi, dünyadan yararlananlar alabildiğine yararlanmıyormuş gibi olsun. Çünkü dünyanın şimdiki hali geçicidir.
Abale, chimene ndikutanthauza nʼchakuti nthawi yatha. Kuyambira tsopano anthu okwatira akhale ngati sanakwatire.
Amene akulira akhale monga ngati sakulira. Amene akukondwa akhale ngati sakukondwa. Amene akugula zinthu akhale ngati alibe zinthuzo.
Amene akugwiritsa ntchito zinthu za dziko lapansi lino, akhale ngati sizikuwakhudza. Pakuti dziko lapansi lino mmene lilirimu, likupita.
32 Kaygısız olmanızı istiyorum. Evli olmayan erkek, Rab'bi nasıl hoşnut edeceğini düşünerek Rab'bin işleri için kaygılanır.
Ine ndikufuna kuti mumasuke ku nkhawa zanu. Munthu wosakwatira amangolabadira za Ambuye, mmene angakondweretsere Ambuyewo.
33 Evli erkekse karısını nasıl hoşnut edeceğini düşünerek dünya işleri için kaygılanır.
Koma wa pa banja amalabadira za dziko lapansi lino, mmene angakondweretsere mkazi wake,
34 Böylece ilgisi bölünür. Evli olmayan kadın ya da kız hem bedence hem ruhça kutsal olmak amacıyla Rab'bin işleri için kaygılanır. Evli kadınsa kocasını nasıl hoşnut edeceğini düşünerek dünya işleri için kaygılanır.
ndipo chifukwa ichi amatanganidwa kwambiri. Mkazi wosakwatiwa kapena namwali, amalabadira za Ambuye. Cholinga chake ndi kudzipereka kwa Ambuye mʼthupi ndi mu uzimu momwe. Koma mkazi wokwatiwa amalabadira za dziko lapansi lino, mmene angakondweretsere mwamuna wake.
35 Bunu sizin iyiliğiniz için söylüyorum, özgürlüğünüzü kısıtlamak için değil. İlginizi dağıtmadan, Rab'be adanmış olarak, O'na yaraşır biçimde yaşamanızı istiyorum.
Ndikunena izi kufuna kuthandiza inu nomwe osati kukupanikizani. Ine ndikufuna mukhale moyenera mosadzigawa pa kudzipereka kwanu kwa Ambuye.
36 Bir kimse nişanlı olduğu kıza yakışıksız davrandığını düşünüyorsa, aşırı tutkuları varsa ve evlenmesi gerekiyorsa, istediğini yapsın, günah işlemiş olmaz; evlensinler.
Ngati wina akuganiza kuti akumulakwira namwali yemwe anapalana naye ubwenzi, ndipo ngati chilakolako chake chikunka chikulirakulirabe, ndipo akuona kuti nʼkofunika kumukwatira, ayenera kuchita monga wafunira, kutero si kuchimwa ayi.
37 Ama zorunluluk altında bulunmayan, yüreği kararlı, istediğini yapabilecek durumdaki kişi, nişanlısıyla evlenmemeye yüreğinde karar vermişse, iyi eder.
Koma ngati wina motsimikiza mtima wake, popanda womukakamiza, koma akuchita mwa chifuniro chake, ndipo watsimikiza mtima kuti samukwatira namwaliyo, munthuyu akuchitanso chokhoza.
38 Kısacası nişanlısıyla evlenen iyi eder, evlenmeyense daha iyi eder.
Choncho amene akukwatira namwali amene ali naye pa ubwenzi, akuchita bwino, koma amene sangakwatire namwaliyo akuchita bwino koposa.
39 Kadın, kocası yaşadıkça kocasına bağlıdır. Kocası ölürse dilediği kimseyle evlenmekte özgürdür; yeter ki, o kişi Rab'be ait biri olsun.
Mkazi amamangika ndi lamulo la ukwati nthawi zonse pamene mwamuna wake ali ndi moyo. Koma mwamuna wake akamwalira, ali ndi ufulu kukwatiwa ndi wina aliyense amene akumufuna, koma mwamunayo akhale wa mwa Ambuye.
40 Ama dul kadın, olduğu gibi kalırsa daha mutlu olur. Ben böyle düşünüyorum ve sanırım bende de Tanrı'nın Ruhu vardır.
Mʼmaganizo anga, mkaziyo adzakhala wokondwa koposa ngati atangokhala wosakwatiwa. Ndipo ndikuganiza kuti inenso ndili naye Mzimu wa Mulungu.

< 1 Korintliler 7 >