< Elçilerin İşleri 11 >

1 Elçilerle bütün Yahudiye'deki kardeşler, öteki ulusların da Tanrı'nın sözünü kabul ettiklerini duydular.
Atumwi ndi abale a ku Yudeya konse anamva kuti anthu a mitundu ina analandiranso Mawu a Mulungu.
2 Ama Petrus Yeruşalim'e gittiği zaman sünnet yanlıları onu eleştirdiler.
Tsono Petro atafika ku Yerusalemu, abale amene anali a mdulidwe anamutsutsa iye,
3 “Sünnetsiz kişilerin evine gidip yemek yemişsin!” dediler.
ndipo anati, “Iwe unalowa mʼnyumba ya anthu osachita mdulidwe ndi kudya nawo.”
4 Petrus baştan başlayarak olanları tek tek onlara anlattı.
Koma Petro anayamba kuwafotokozera zonse mwatsatanetsatane momwe zinachitikira kuti,
5 “Ben Yafa Kenti'nde dua ediyordum” dedi. “Kendimden geçerek bir görüm gördüm. Büyük bir çarşafı andıran bir nesnenin dört köşesinden sarkıtıldığını, bunun gökten inip benim bulunduğum yere kadar geldiğini gördüm.
“Ine ndimapemphera mu mzinda wa Yopa ndipo ndili ngati wokomoka ndinaona masomphenya. Ndinaona chinthu chokhala ngati chinsalu chachikulu chikutsika kuchokera kumwamba chogwiridwa msonga zake zinayi, ndipo chinatsikira pa ine.
6 Gözlerimi çarşafa dikip dikkatle baktım. Çarşafın içinde, yeryüzünde yaşayan dört ayaklılar, yabanıl hayvanlar, sürüngenler ve kuşlar gördüm.
Ine ndinayangʼana mʼkati mwake ndipo ndinaona nyama za miyendo inayi za mʼdziko lapansi, zirombo, zokwawa, ndi mbalame zamlengalenga.
7 Sonra bir sesin bana, ‘Kalk, Petrus, kes ve ye!’ dediğini işittim.
Kenaka ine ndinamva mawu akuti, ‘Petro, Imirira. Ipha, nudye.’
8 “‘Asla olmaz, ya Rab!’ dedim. ‘Ağzıma hiçbir zaman bayağı ya da murdar bir şey girmedi.’
“Ine ndinayankha kuti, ‘Ayi, Ambuye! Pakuti chinthu chodetsedwa ndi chonyansa sindinadyepo pakamwa pangapa.’
9 “Ses ikinci kez gökten geldi: ‘Tanrı'nın temiz kıldıklarına sen bayağı deme’ dedi.
“Mawu ochokera kumwamba ananenanso kachiwiri kuti, ‘Chimene Mulungu wachiyeretsa usanene kuti ndi chodetsedwa.’
10 Bu, üç kez tekrarlandı; sonra her şey yeniden göğe alındı.
Zimenezi zinachitika katatu ndipo kenaka zonse zinatengedwa kupita kumwamba.
11 “Tam o sırada Sezariye'den bana gönderilen üç kişi, bulunduğumuz evin önünde durdular.
“Nthawi yomweyo anthu atatu amene anatumidwa kuchokera ku Kaisareya anayima pa nyumba yomwe ndimakhalayo.
12 Ruh bana, ayrım gözetmeden onlarla birlikte gitmemi söyledi. Bu altı kardeş de benimle geldiler, varıp adamın evine girdik.
Mzimu anandiwuza kuti ndisakayike, koma ndipite nawo. Abale asanu ndi mmodzi awa anapitanso nane ndipo tinalowa mʼnyumba ya munthuyo.
13 Adam bize, evinde beliren meleği nasıl gördüğünü anlattı. Melek ona şöyle demiş: ‘Yafa'ya adam yolla, Petrus diye tanınan Simun'u çağırt.
Iye anatiwuza mmene anaonera mngelo atayimirira mʼnyumba mwake ndi kumuwuza kuti, ‘Tumiza anthu ku Yopa kuti akayitane Simoni wotchedwa Petro.
14 O sana, senin ve bütün ev halkının kurtuluş bulacağı sözler söyleyecek.’
Iye adzakuwuza uthenga umene udzapulumutsa iwe ndi a pa banja ako.’
15 “Ben konuşmaya başlayınca Kutsal Ruh, başlangıçta bizim üzerimize indiği gibi, onların da üzerine indi.
“Nditangoyamba kuyankhula, Mzimu Woyera anafika pa iwo monga momwe anafikira pa ife poyamba paja.
16 O zaman Rab'bin söylediği şu sözü anımsadım: ‘Yahya suyla vaftiz etti, sizler ise Kutsal Ruh'la vaftiz edileceksiniz.’
Kenaka ndinakumbukira zimene Ambuye ananena kuti, ‘Yohane anabatiza ndi madzi, koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.’
17 Böylelikle Tanrı, Rab İsa Mesih'e inanmış olan bizlere verdiği armağanın aynısını onlara verdiyse, ben kimim ki Tanrı'ya karşı koyayım?”
Tsono ngati Mulungu anawapatsa iwo mphatso yomweyo imene anatipatsa ife, amene tinakhulupirira Ambuye Yesu Khristu, ndine yani kuti nditsutsane ndi Mulungu?”
18 Bunları dinledikten sonra yatıştılar. Tanrı'yı yücelterek şöyle dediler: “Demek ki Tanrı, tövbe etme ve yaşama kavuşma fırsatını öteki uluslara da vermiştir.”
Iwo atamva zimenezi analibenso chonena ndipo anayamika Mulungu nati, “Potero Mulungu wapatsa anthu a mitundu ina mwayi wotembenuka mtima ndi kulandira moyo.”
19 İstefanos'un öldürülmesiyle başlayan baskı sonucu dağılan imanlılar, Fenike, Kıbrıs ve Antakya'ya kadar gittiler. Tanrı sözünü sadece Yahudiler'e duyuruyorlardı.
Tsopano amene anabalalika chifukwa cha mazunzo amene anayamba ataphedwa Stefano, anapita mpaka ku Foinike, ku Kupro ndi ku Antiokeya, ndipo ankalalikira kwa Ayuda okha.
20 Ama içlerinden Kıbrıslı ve Kireneli olan bazı adamlar Antakya'ya gidip Grekler'le de konuşmaya başladılar. Onlara Rab İsa'yla ilgili Müjde'yi bildirdiler.
Komabe, ena pakati pawo ochokera ku Kupro ndi ku Kurene anapita ku Antiokeya ndipo iwo anayamba kuyankhulanso kwa Agriki, nawawuza za Uthenga Wabwino wa Ambuye Yesu.
21 Onların arasında etkin olan Rab'bin gücü sayesinde çok sayıda kişi inanıp Rab'be döndü.
Mphamvu ya Ambuye inali nawo ndipo anthu ambiri anakhulupirira natembenukira kwa Ambuye.
22 Olup bitenlerin haberi, Yeruşalim'deki kiliseye ulaştı. Bunun üzerine imanlılar Barnaba'yı Antakya'ya gönderdiler.
Mbiri imeneyi inamveka ku mpingo wa ku Yerusalemu ndipo iwo anatumiza Barnaba ku Antiokeya.
23 Kutsal Ruh'la ve imanla dolu, iyi bir adam olan Barnaba, Antakya'ya varıp Tanrı lütfunun meyvelerini görünce sevindi. Herkesi, candan ve yürekten Rab'be bağlı kalmaya özendirdi. Sonuç olarak Rab'be daha birçok kişi kazanıldı.
Atafika ndi kuona chisomo cha Mulungu pa iwo, anakondwa ndi kuwalimbikitsa anthu onsewo kuti apitirire kukhala woona mu mtima mwa Ambuye.
Barnabayo anali munthu wabwino, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi chikhulupiriro ndipo gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Ambuye.
25 Sonra Barnaba, Saul'u aramak için Tarsus'a gitti. Onu bulunca da Antakya'ya getirdi. Böylece Barnaba'yla Saul bir yıl boyunca oradaki inanlılar topluluğuyla bir araya gelerek büyük bir kitleyi eğittiler. Öğrencilere ilk kez Antakya'da Mesihçiler adı verildi.
Kenaka Barnaba anapita ku Tarisisi kukafuna Saulo,
ndipo pamene anamupeza anabwera naye ku Antiokeya. Barnaba ndi Saulo anasonkhana ndi mpingo kwa chaka chimodzi naphunzitsa anthu ambirimbiri. Okhulupirirawo anayamba kutchedwa Akhristu ku Antiokeya.
27 O günlerde Yeruşalim'den Antakya'ya bazı peygamberler geldi.
Masiku amenewo ku Antiokeya kunafika aneneri ena ochokera ku Yerusalemu.
28 Bunlardan Hagavos adlı biri ortaya çıkıp bütün dünyada şiddetli bir kıtlık olacağını Ruh aracılığıyla bildirdi. Bu kıtlık, Klavdius'un imparatorluğu sırasında oldu.
Mmodzi wa iwo dzina lake Agabu, anayimirira ndipo Mzimu anamutsogolera kunenera zamʼtsogolo kuti padzakhala njala yayikulu pa dziko lonse lapansi. (Izi zinachitikadi nthawi ya ulamuliro wa Klaudiyo).
29 Öğrenciler, her biri kendi gücü oranında, Yahudiye'de yaşayan kardeşlere gönderilmek üzere yardım toplamayı kararlaştırdılar.
Ophunzirawo, aliyense monga mwakupata kwake, anatsimikiza kuthandiza abale okhala ku Yudeya.
30 Bu kararı yerine getirip bağışlarını Barnaba ve Saul'un eliyle kilisenin ihtiyarlarına gönderdiler.
Izi anazichitadi ndipo anatuma Barnaba ndi Saulo kukapereka mphatsozo kwa akulu a mpingo.

< Elçilerin İşleri 11 >