< Hezekiel 27 >

1 RAB bana şöyle seslendi:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 “İnsanoğlu, Sur Kenti için bir ağıt yak.
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
3 Denizin kıyısında kurulmuş, kıyı halklarıyla ticaret yapan Sur Kenti'ne de ki, ‘Egemen RAB şöyle diyor: “‘Ey Sur, güzellikte kusursuzum dedin.
Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
4 Sınırların denizin bağrındaydı, Kurucuların güzelliğini doruğa ulaştırdılar.
Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
5 Bütün kerestelerini Senir'in çam ağaçlarından yaptılar, Sana direk yapmak için Lübnan'dan sedir ağaçları aldılar.
Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
6 Küreklerini Başan meşelerinden, Güverteni Kittim kıyılarından getirilen Selvi ağaçlarından yaptılar, Fildişiyle süslediler.
Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
7 Mısır'ın işlemeli ince keteninden yelkenin, Bayrağın oldu senin. Güvertenin gölgeliği Elişa kıyılarının Lacivert, mor kumaşındandı.
Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
8 Kürekçilerin Saydalı ve Arvatlı'ydı, Gemicilerin, içindeki becerikli kişilerdi, ey Sur.
Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
9 Gemilerindeki gedikleri onaranlar Geval'ın deneyimli, usta adamlarıydı. Denizdeki bütün gemiler ve denizciler Mallarını değiş tokuş etmek için sana geldiler.
Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
10 Persli, Ludlu, Pûtlu askerler Ordunda hizmet etti. Kalkanlarını, miğferlerini Duvarlarına astılar, Sana görkem kazandırdılar.
“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
11 Arvat'tan, Helek'ten gelen adamlar Çepeçevre duvarlarını korudular. Gammat'tan gelen adamlar Kulelerinde beklediler. Kalkanlarını duvarlarına astılar. Güzelliğini doruğa ulaştırdılar.
Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
12 “‘Tarşiş seninle ticaret yaptı, Sende her çeşit mal vardı. Mallarına karşılık Sana gümüş, demir, kalay, kurşun verdiler.
“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
13 Yâvan, Tuval, Meşek seninle ticaret yaptı, Mallarına karşılık Sana köle ve tunç kaplar verdiler.
“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
14 Beyttogarma halkı Mallarına karşılık Sana at, savaş atı, katır verdi.
“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
15 Rodos halkı seninle ticaret yaptı. Birçok kıyı halkı senin müşterindi. Senden aldıkları mala karşılık Fildişi ve abanoz verdiler.
“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
16 Sende çok çeşit ürün olduğundan, Edom seninle ticaret yaptı. Mallarına karşılık Sana firuze, mor kumaş, işlemeli giysiler, İnce keten, mercan, yakut verdiler.
“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
17 Yahuda ve İsrail seninle ticaret yaptı. Mallarına karşılık Sana Minnit buğdayı, darı, bal, zeytinyağı, pelesenk verdiler.
“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
18 Ürünlerinin çeşitliliği, malının bolluğundan ötürü Şam seninle ticaret yaptı. Mallarına karşılık Sana Helbon şarabıyla Sahar yünü, Uzal'dan getirilmiş şarap tekneleri verdi. Sana getirilen mallar arasında İşlenmiş demir, tarçın, güzel kokulu kamış vardı.
“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
20 Dedan halkı mallarına karşılık Sana eyerlik kumaş verdi.
“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
21 Arabistan ve Kedar önderleri müşterindi, Mallarına karşılık Sana kuzu, koç, teke verdiler.
“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
22 Saba ve Raama tüccarları seninle ticaret yaptı, Mallarına karşılık Sana her çeşit baharatın en iyisini, değerli taşlar, altın verdiler.
“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
23 Harran, Kanne, Eden, Saba, Aşur, Kilmat tüccarları Seninle ticaret yaptı.
“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
24 Pazarlarındaki mallara karşılık Güzel giysiler, lacivert kumaş, işlemeler, Sık dokunmuş, iplerle sarılmış renkli halılar verdiler.
Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
25 Ticaret gemileri senin mallarını taşıdı, Denizin bağrında büyük yükle doldun.
“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
26 Kürekçilerin seni açık denizlere götürdü, Ama doğu rüzgarı Denizin bağrında parçaladı seni.
Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
27 Gemin kazaya uğrayacağı gün, Zenginliğin, malların, ticari eşyaların, Gemicilerin, kılavuzların, kalafatçıların, Seninle ticaret yapanlar, Askerlerin ve gemide olan herkes Denizin derinliklerine batacak.
Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
28 Gemicilerinin bağırışından Kıyılar titreyecek.
Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
29 Kürekçiler gemilerini bırakacak, Gemicilerle kılavuzlar kıyıda duracak.
Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
30 Yüksek sesle haykırıp Senin için acı acı ağlayacaklar; Başlarına toprak serpecek, Külde yuvarlanacaklar.
Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
31 Senin yüzünden başlarını tıraş edecek, Çul kuşanacaklar. Senin için acı acı ağlayacak, Yas tutacaklar.
Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
32 Ağlayıp yas tutarken, Senin için bir ağıt yakacaklar: Her yanı denizle çevrili Sur Kenti gibi Susturulmuş bir kent var mı?
Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
33 Malların denizaşırı ülkelere vardığında Birçok ulusu doyurdun, Büyük zenginliğin, çeşit çeşit malınla Dünya krallarını zenginleştirdin.
Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
34 Şimdiyse denizde, suların derinliklerinde Darmadağın oldun, Malların ve çalışanlarının tümü Seninle birlikte battı.
Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
35 Kıyı halkları Başına gelenlere şaştılar; Krallarının tüyleri korkudan diken diken oldu, Yüzleri sarardı.
Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
36 Ulusların arasındaki tüccarlar, Başına gelenlere şaşacaklar; Sonun korkunç oldu. Bir daha var olmayacaksın.’”
Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”

< Hezekiel 27 >