< İbraniler 12 >

1 İşte çevremizi bu denli büyük bir tanıklar bulutu sardığına göre, biz de her yükü ve bizi kolayca kuşatan günahı üzerimizden sıyırıp atalım ve önümüze konan yarışı sabırla koşalım.
Tsono popeza ifenso tazunguliridwa ndi gulu lalikulu la mboni, tiyeni titaye chilichonse chimene chimatitchinga, makamaka tchimo limene limatikola mosavuta, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu.
2 Gözümüzü imanımızın öncüsü ve tamamlayıcısı İsa'ya dikelim. O kendisini bekleyen sevinç uğruna utancı hiçe sayıp çarmıhta ölüme katlandı ve şimdi Tanrı'nın tahtının sağında oturuyor.
Tiyeni tiyangʼanitsitse Yesu, amene ndi woyamba ndi wotsiriza wa chikhulupiriro chathu. Chifukwa cha chimwemwe chimene chimamudikira anapirira zowawa zapamtanda. Iye ananyoza manyazi a imfa yotere ndipo tsopano akukhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu.
3 Yorulup cesaretinizi yitirmemek için, günahkârların bunca karşı koymasına katlanmış Olan'ı düşünün.
Muzilingalira za Iye amene anapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafowoke ndi kutaya mtima.
4 Günaha karşı verdiğiniz mücadelede henüz kanınızı akıtacak kadar direnmiş değilsiniz.
Polimbana ndi uchimo, simunafike mpaka pokhetsa magazi.
5 Size oğullar diye seslenen şu öğüdü de unuttunuz: “Oğlum, Rab'bin terbiye edişini hafife alma, Rab seni azarlayınca cesaretini yitirme.
Kodi mwayiwala mawu olimbitsa mtima aja, amene Mulungu anayankhula kwa inu ngati ana ake? Mawuwo ndi awa: “Mwana wanga, usapeputse kulanga kwa Ambuye ndipo usataye mtima pamene akukudzudzula.
6 Çünkü Rab sevdiğini terbiye eder, Oğulluğa kabul ettiği herkesi cezalandırır.”
Chifukwa Ambuye amadzudzula amene amawakonda ndipo amalanga aliyense amene amamulandira.”
7 Terbiye edilmek uğruna acılara katlanmalısınız. Tanrı size oğullarına davranır gibi davranıyor. Hangi oğul babası tarafından terbiye edilmez?
Pamene mukupirira masautso monga chilango, Mulungu achitira inu monga ana ake. Kodi ndi mwana wotani amene abambo ake samulanga?
8 Herkesin gördüğü terbiyeden yoksunsanız, oğullar değil, yasadışı evlatlarsınız.
Ngati inu simulangidwa, komatu aliyense amalangidwa, ndiye kuti sindinu ana enieni koma amʼchigololo.
9 Kaldı ki, bizi terbiye eden dünyasal babalarımız vardı ve onlara saygı duyardık. Öyleyse Ruhlar Babası'na bağımlı olup yaşamamız çok daha önemli değil mi?
Komanso, tonsefe tinali ndi abambo athu otibala amene amatilanga ndipo timawapatsa ulemu. Nanga kodi sitidzagonjera Atate a mizimu yathu kuti tikhale ndi moyo?
10 Babalarımız bizi kısa bir süre için, uygun gördükleri gibi terbiye ettiler. Ama Tanrı, kutsallığına ortak olalım diye bizi kendi yararımıza terbiye ediyor.
Abambo athu ankatilanga kwa kanthawi kochepa monga amaonera kufunika kwake, koma Mulungu amatilanga kuti tipindule, kuti tikhale oyera mtima.
11 Terbiye edilmek başlangıçta hiç tatlı gelmez, acı gelir. Ne var ki, böyle eğitilenler için bu sonradan esenlik veren doğruluğu üretir.
Palibe chilango chimene chimaoneka kuti ndi chabwino pa nthawiyo, komatu chowawa. Koma pambuyo pake, chimabweretsa chipatso chachilungamo ndi mtendere kwa iwo amene aleredwa mwa njira imeneyi.
12 Bunun için sarkık ellerinizi kaldırın, bükük dizlerinizi doğrultun, ayaklarınız için düz yollar yapın. Öyle ki, kötürüm olan parça eklemden çıkmasın, tersine şifa bulsun.
Nʼchifukwa chake limbitsani manja anu otopa ndi mawondo anu ogowoka.
Muziyenda mʼnjira zowongoka, kuti iwo amene akukutsatirani ngakhale ndi olumala ndi ofowoka asapunthwe ndi kugwa koma adzilimbikitsidwa.
14 Herkesle barış içinde yaşamaya, kutsal olmaya gayret edin. Kutsallığa sahip olmadan kimse Rab'bi göremeyecek.
Yesetsani kukhala pa mtendere ndi anthu onse ndi kukhala oyera mtima, pakuti popanda chiyero palibe ndi mmodzi yemwe adzaona Ambuye.
15 Dikkat edin, kimse Tanrı'nın lütfundan yoksun kalmasın. İçinizde sizi rahatsız edecek ve birçoklarını zehirleyecek acı bir kök filizlenmesin.
Yangʼanitsitsani kuti wina aliyense asachiphonye chisomo cha Mulungu ndiponso kuti pasaphuke muzu wamkwiyo umene udzabweretsa mavuto ndi kudetsa ambiri.
16 Kimse fuhuş yapmasın ya da ilk oğulluk hakkını bir yemeğe karşılık satan Esav gibi kutsal değerlere saygısızlık etmesin.
Yangʼanitsitsani kuti pasakhale wina wachigololo. Kapena wosapembedza ngati Esau, amene chifukwa cha chakudya cha kamodzi kokha anagulitsa ukulu wake.
17 Biliyorsunuz, Esav daha sonra kutsanma hakkını miras almak istediyse de geri çevrildi. Kutsanmak için gözyaşı döküp yalvarmasına karşın, vermiş olduğu kararın sonucunu değiştiremedi.
Monga inu mukudziwa, pambuyo pake pamene anafuna kuti adalitsidwe anakanidwa. Sanapezenso mpata woti asinthe maganizo, ngakhale anafuna madalitsowo ndi misozi.
18 Sizler dokunulabilen, alev alev yanan dağa, karanlığa, koyu karanlık ve kasırgaya, gürleyen çağrı borusuna, tanrısal sözleri ileten sese yaklaşmış değilsiniz. O sesi işitenler, kendilerine bir sözcük daha söylenmesin diye yalvardılar.
Inu simunafike ku phiri limene mungathe kulikhudza, loyaka moto wa mdima bii, la mphepo yamkuntho;
limene pali kulira kwa lipenga, ndiponso kumveka kwa mawu. Anthu amene amamva mawuwo anapempha kuti asawayankhulenso mawu ena.
20 “Dağa bir hayvan bile dokunsa taşlanacak” buyruğuna dayanamadılar.
Iwo anachita mantha ndi lamulo lija lakuti, “Ngakhale nyama ikangokhudza phirilo, iphedwe ndi miyala.”
21 Görünüm öyle korkunçtu ki, Musa, “Çok korkuyorum, titriyorum” dedi.
Maonekedwenso a Mose anali woopsa kwambiri, ngakhale Mose yemwe anati, “Ine ndinachita mantha ndi kunjenjemera.”
22 Oysa sizler Siyon Dağı'na, yaşayan Tanrı'nın kenti olan göksel Yeruşalim'e, bir bayram şenliği içindeki on binlerce meleğe, adları göklerde yazılmış ilk doğanların topluluğuna yaklaştınız. Herkesin yargıcı olan Tanrı'ya, yetkinliğe erdirilmiş doğru kişilerin ruhlarına, yeni antlaşmanın aracısı olan İsa'ya ve Habil'in kanından daha üstün bir anlam taşıyan serpmelik kana yaklaştınız.
Koma inu mwafika ku Phiri la Ziyoni, ku mzinda wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wakumwamba. Mwafika mu msonkhano wa angelo osangalala osawerengeka.
Mwafika mu mpingo wa ana oyamba kubadwa, amene mayina awo analembedwa kumwamba. Inu mwafika kwa Mulungu, woweruza anthu onse, ndiponso kwa mizimu ya anthu olungama ndi osandutsidwa kukhala angwiro.
Kwa Yesu mʼkhalapakati wa pangano latsopano, ndiponso mwafika ku magazi owazidwa amene amayankhula mawu abwino kuposa magazi a Abele.
25 Bunları söyleyeni reddetmemeye dikkat edin. Çünkü yeryüzünde kendilerini uyaranı reddedenler kurtulamadılarsa, göklerden bizi uyarandan yüz çevirirsek, bizim de kurtulamayacağımız çok daha kesindir.
Chenjerani kuti musakane kumvera amene akuyankhula nanu. Anthu amene anakana kumvera iye amene anawachenjeza uja pa dziko lapansi pano, sanapulumuke ku chilango ayi, nanga tsono ife tidzapulumuka bwanji ngati tikufulatira wotichenjeza wochokera kumwamba?
26 O zaman O'nun sesi yeri sarsmıştı. Ama şimdi, “Bir kez daha yalnız yeri değil, göğü de sarsacağım” diye söz vermiştir.
Pa nthawiyo mawu ake anagwedeza dziko lapansi, koma tsopano Iye walonjeza kuti, “Kamodzi kenanso ndidzagwedeza osati dziko lapansi lokha komanso thambo.”
27 “Bir kez daha” sözü, sarsılanların, yani yaratılmış olan şeylerin ortadan kaldırılacağını, böylelikle sarsılmayanların kalacağını anlatıyor.
Mawu akuti, “Kamodzi kenanso,” akuonetsa kuchotsedwa kwa zimene zitha kugwedezeka, zonse zolengedwa, kotero kuti zimene sizingatheke kugwedezeka zitsale.
28 Böylece sarsılmaz bir egemenliğe kavuştuğumuz için minnettar olalım. Öyle ki, Tanrı'yı hoşnut edecek biçimde saygı ve korkuyla tapınalım.
Popeza tikulandira ufumu umene sungagwedezeke, tiyeni tikhale oyamika ndi kupembedza Mulungu movomerezeka ndi mwaulemu ndi mantha.
29 Çünkü Tanrımız yakıp yok eden bir ateştir.
Pakuti Mulungu wathu ndi moto wonyeketsa.

< İbraniler 12 >