< Yeşu 2 >

1 Nun oğlu Yeşu Şittim'den gizlice iki casus gönderdi. “Gidip ülkeyi, özellikle de Eriha'yı araştırın” dedi. Böylece yola çıkan casuslar, Rahav adında bir fahişenin evine gidip geceyi orada geçirdiler.
Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.
2 Bu arada Eriha Kralı'na, “Ülkemizi araştırmak üzere bu gece İsrail halkından buraya adamlar geldi” diye haber verildi.
Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.”
3 Bunun üzerine Eriha Kralı, Rahav'a, “Sana gelip evinde kalan o adamları dışarı çıkar” diye haber gönderdi, “Çünkü onlar ülkemizi araştırmak için geldiler.”
Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”
4 İki adamı saklamış olan Rahav, “Adamların bana geldikleri doğru” dedi, “Ama ben nereli olduklarını bilmiyordum.
Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera.
5 Karanlık basar basmaz, kentin kapısı kapanmak üzereyken çıktılar. Nereye gittiklerini bilmiyorum. Hemen peşlerinden giderseniz yetişirsiniz.”
Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.”
6 Aslında kadın onları dama çıkarmış, oraya sermiş olduğu keten saplarının altına gizlemişti.
Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo.
7 Kralın adamlarıysa casusları Şeria Irmağı'nın geçitlerine giden yol boyunca kovaladılar. Onlar kentten çıkar çıkmaz kapı sürgülenmişti.
Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.
8 Damdaki adamlar yatmadan önce kadın yanlarına çıktı.
Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga
9 “RAB'bin bu ülkeyi size verdiğini biliyorum” dedi, “Sizden ötürü dehşete kapıldık; ülkede yaşayan herkesin korkudan dizlerinin bağı çözüldü.
ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu.
10 Çünkü Mısır'dan çıktığınızda RAB'bin Kamış Denizi'ni önünüzde nasıl kuruttuğunu, Şeria Irmağı'nın ötesindeki Amorlu iki krala –Sihon ve Og'a– neler yaptığınızı, onları nasıl yok ettiğinizi duyduk.
Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu.
11 Bunları duyduğumuzda korkudan dizlerimizin bağı çözüldü. Sizin korkunuzdan kimsede derman kalmadı. Çünkü Tanrınız RAB hem yukarıda göklerde, hem de aşağıda yeryüzünde Tanrı'dır.
Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi.
12 Size iyilik ettiğim gibi, siz de aileme iyilik edeceğinize lütfen RAB adına ant için. Annemi, babamı, erkek ve kız kardeşlerimle ailelerini ölümden kurtarıp hepimizi sağ bırakacağınıza ilişkin bana güvenilir bir işaret verin.”
Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga.
Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”
14 Adamlar, “Eğer bu yaptıklarımızı açığa vurmazsanız, yerinize ölmeye hazırız” dediler, “RAB bu ülkeyi bize verdiğinde sana iyilik edip sözümüzü tutacağız.”
Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”
15 Kent surlarında bir evde oturan Rahav, adamları iple pencereden aşağı indirdi.
Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe.
16 Onlara, “Dağa çıkın, yoksa sizi kovalayanlarla karşılaşabilirsiniz” dedi, “Onlar dönene kadar üç gün orada saklanın. Sonra yolunuza devam edersiniz.”
Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”
17 Adamlar Rahav'a, “Bize içirdiğin andı tutmasına tutarız” dediler,
Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi
18 “Ama ülkeye girdiğimizde şu kırmızı ipi bizi indirdiğin pencereye bağla. Anneni, babanı, kardeşlerinle babanın bütün ev halkını yanına, kendi evine topla.
tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno.
19 Evinin kapısından dışarıya çıkan, kendi kanından sorumlu olacak; böyle biri için sorumluluk kabul etmeyiz. Ama seninle birlikte evinde olan herhangi birine gelecek zarardan biz sorumluyuz.
Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu.
20 Ancak bu yaptıklarımızı açığa vurursan, içirdiğin ant bizi bağlamaz.”
Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”
21 Kadın, “Dediğiniz gibi olsun” diye karşılık verdi. Onları yola çıkarıp uğurladıktan sonra kırmızı ipi pencereye bağladı.
Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.
22 Adamlar ayrılıp dağa çıktılar; kendilerini kovalayanlar dönünceye dek üç gün orada kaldılar. Kovalayanlar yol boyu onları aradılarsa da bulamadılar.
Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza.
23 İki adam geri dönmek üzere dağdan indi. Irmağı geçip Nun oğlu Yeşu'nun yanına vardılar ve başlarından geçen her şeyi ona anlattılar.
Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira.
24 Yeşu'ya, “RAB gerçekten bütün ülkeyi elimize teslim etti” dediler, “Orada yaşayan herkesin korkudan dizlerinin bağı çözüldü.”
Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”

< Yeşu 2 >