< Luka 21 >

1 İsa başını kaldırdı ve bağış toplanan yerde bağışlarını bırakan zenginleri gördü.
Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu.
2 Yoksul bir dul kadının oraya iki bakır para attığını görünce, “Size gerçeği söyleyeyim” dedi, “Bu yoksul dul kadın herkesten daha çok verdi.
Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri.
3
Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa.
4 Çünkü bunların hepsi kutuya, zenginliklerinden artanı attılar. Bu kadın ise yoksulluğuna karşın, geçinmek için elinde ne varsa hepsini verdi.”
Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
5 Bazı kişiler tapınağın nasıl güzel taşlar ve adaklarla süslenmiş olduğundan söz edince İsa, “Burada gördüklerinize gelince, öyle günler gelecek ki, taş üstünde taş kalmayacak, hepsi yıkılacak!” dedi.
Ena mwa ophunzira ake ankachita ndemanga za mmene Nyumba ya Mulungu anayikongoletsera ndi miyala yokongola ndiponso zinthu zina zomwe anthu anapereka kwa Mulungu. Koma Yesu anati,
6
“Koma zimene mukuziona panozi, nthawi idzafika pamene ngakhale mwala umodzi omwe sudzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
7 Onlar da, “Peki, öğretmenimiz, bu dediklerin ne zaman olacak? Bunların gerçekleşmek üzere olduğunu gösteren belirti ne olacak?” diye sordular.
Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi zonsezi zidzachitika liti? Ndipo tidzaonera chiyani kuti zili pafupi kuchitika?”
8 İsa, “Sakın sizi saptırmasınlar” dedi. “Birçokları, ‘Ben O'yum’ ve ‘Zaman yaklaştı’ diyerek benim adımla gelecekler. Onların ardından gitmeyin.
Iye anayankha kuti, “Chenjerani kuti musanyengedwe. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati ‘Ine ndine Iye’ ndi kuti ‘Nthawi yayandikira.’ Musadzawatsate iwo.
9 Savaş ve isyan haberleri duyunca telaşlanmayın. Önce bunların olması gerek, ama son hemen gelmeyecek.”
Mukadzamva zankhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha. Zinthu izi ziyenera kuchitika poyamba, koma chimaliziro sichidzafika nthawi yomweyo.”
10 Sonra onlara şöyle dedi: “Ulus ulusa, devlet devlete savaş açacak.
Kenaka anawawuza kuti, “Mtundu wa anthu udzawukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu kuwukira ufumu wina.
11 Şiddetli depremler, yer yer kıtlıklar ve salgın hastalıklar, korkunç olaylar ve gökte olağanüstü belirtiler olacak.
Kudzakhala zivomerezi zazikulu, njala ndi miliri mʼmalo osiyanasiyana, ndi zinthu zoopsa ndi zizindikiro zamphamvu kuchokera kumwamba.
12 “Ama bütün bu olaylardan önce sizi yakalayıp zulmedecekler. Sizi havralara teslim edecek, zindanlara atacaklar. Benim adımdan ötürü kralların, valilerin önüne çıkarılacaksınız.
“Koma zonsezi zisanachitike, adzakugwirani ndi kukuzunzani. Adzakuperekani ku masunagoge ndi ku ndende, ndipo adzakutengerani pamaso pa mafumu ndi olamulira, ndipo zonsezi zidzachitika chifukwa cha dzina langa.
13 Bu size tanıklık etme fırsatı olacak.
Umenewu udzakhala mwayi wanu ochitira umboni.
14 Buna göre kendinizi nasıl savunacağınızı önceden düşünmemekte kararlı olun.
Koma tsimikizani mtima kuti musadzade nkhawa za momwe mudzadzitchinjirizire.
15 Çünkü ben size öyle bir konuşma yeteneği, öyle bir bilgelik vereceğim ki, size karşı çıkanların hiçbiri buna karşı direnemeyecek, bir şey diyemeyecek.
Pakuti Ine ndidzakupatsani mawu ndi nzeru kotero kuti palibe mmodzi wa adani anu adzathe kuwakana kapena kuwatsutsa.
16 Anne babanız, kardeşleriniz, akraba ve dostlarınız bile sizi ele verecek ve bazılarınızı öldürtecekler.
Inu mudzaperekedwa ndi makolo anu, abale, anansi ndi abwenzi anu ndipo ena mwa inu adzakuphani.
17 Benim adımdan ötürü herkes sizden nefret edecek.
Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine.
18 Ne var ki, başınızdaki saçlardan bir tel bile yok olmayacaktır.
Koma palibe tsitsi limodzi la mʼmutu mwanu lidzawonongeke.
19 Dayanmakla canlarınızı kazanacaksınız.
Mukadzalimbikira ndiye mudzapeze moyo.
20 “Yeruşalim'in ordular tarafından kuşatıldığını görünce bilin ki, kentin yıkılacağı zaman yaklaşmıştır.
“Mukadzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu ankhondo, inu mudzadziwe kuti kuwonongeka kwake kuli pafupi.
21 O zaman Yahudiye'de bulunanlar dağlara kaçsın, kentte olanlar dışarı çıksın, kırdakiler kente dönmesin.
Pamenepo amene ali ku Yudeya adzathawire ku mapiri, amene ali mu mzinda adzatulukemo, ndi amene ali ku midzi asadzalowe mu mzinda.
22 Çünkü o günler, yazılmış olanların tümünün gerçekleşeceği ceza günleridir.
Pakuti iyi ndi nthawi yachilango pokwaniritsa zonse zimene zinalembedwa.
23 O günlerde gebe olan, çocuk emziren kadınların vay haline! Çünkü ülke büyük sıkıntıya düşecek ve bu halk gazaba uğrayacaktır.
Zidzakhala zoopsa nthawi imenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! Kudzakhala masautso aakulu mʼdziko ndipo anthu onse adzawakwiyira.
24 Kılıçtan geçirilecek, tutsak olarak bütün uluslar arasına sürülecekler. Yeruşalim, öteki ulusların dönemleri tamamlanıncaya dek onların ayakları altında çiğnenecektir.
Iwo adzaphedwa ndi lupanga ndi kutengedwa ukapolo kupita ku mayiko wonse. Yerusalemu adzaponderezedwa ndi anthu a mitundu ina mpaka nthawi ya a mitundu ina itakwaniritsidwa.
25 “Güneşte, ayda ve yıldızlarda belirtiler görülecek. Yeryüzünde uluslar denizin ve dalgaların uğultusundan şaşkına dönecek, dehşete düşecekler.
“Padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, mwezi ndi nyenyezi. Pa dziko lapansi, mitundu ya anthu idzakhala mʼmasautso ndipo idzathedwa nzeru pakumva mkokomo ndi mafunde a mʼnyanja.
26 Dünyanın üzerine gelecek felaketleri bekleyen insanlar korkudan bayılacak. Çünkü göksel güçler sarsılacak.
Anthu adzakomoka chifukwa cha mantha, akadzamva za zimene zikubwera pa dziko lapansi, pakuti zinthu zamlengalenga zidzagwedezeka.
27 O zaman İnsanoğlu'nun bulut içinde büyük güç ve görkemle geldiğini görecekler.
Nthawi imeneyo adzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
28 Bu olaylar gerçekleşmeye başlayınca doğrulun ve başlarınızı kaldırın. Çünkü kurtuluşunuz yakın demektir.”
Zinthu izi zikadzayamba kuchitika, mudzayimirire ndi kutukula mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira.”
29 İsa onlara şu benzetmeyi anlattı: “İncir ağacına ya da herhangi bir ağaca bakın.
Iye anawawuza fanizo ili, “Taonani mtengo wamkuyu ndi mitengo ina yonse.
30 Bunların yapraklandığını gördüğünüz zaman yaz mevsiminin yakın olduğunu kendiliğinizden anlarsınız.
Ikamatulutsa masamba, mumakhoza kudzionera nokha ndi kudziwa kuti dzinja lili pafupi.
31 Aynı şekilde, bu olayların gerçekleştiğini gördüğünüzde bilin ki, Tanrı'nın Egemenliği yakındır.
Chimodzimodzinso, mukadzaona zinthu zonsezi, dziwani kuti ufumu wa Mulungu uli pafupi.
32 Size doğrusunu söyleyeyim, bütün bunlar olmadan, bu kuşak ortadan kalkmayacak.
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
33 Yer ve gök ortadan kalkacak, ama benim sözlerim asla ortadan kalkmayacaktır.
Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
34 “Kendinize dikkat edin! Yürekleriniz sefahat, sarhoşluk ve bu yaşamın kaygılarıyla ağırlaşmasın. O gün, üzerinize bir tuzak gibi aniden inmesin. Çünkü o gün bütün yeryüzünde yaşayan herkesin üzerine gelecektir.
“Samalani, kuti mitima yanu ingalemetsedwe ndi maphwando, kuledzera ndi kudera nkhawa za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingadzakupezeni modzidzimutsa ngati msampha.
Pakuti lidzafika pa onse okhala pa dziko lonse lapansi.
36 Her an uyanık kalın, gerçekleşmek üzere olan bütün bu olaylardan kurtulabilmek ve İnsanoğlu'nun önünde durabilmek için dua edin.”
Khalani tcheru nthawi zonse ndi kupemphera kuti inu mudzathe kuthawa zonse zimene zili pafupi kuchitika, ndi kuti mudzathe kuyima pamaso pa Mwana wa Munthu.”
37 İsa gündüz tapınakta öğretiyor, geceleri ise kentten dışarı çıkıp Zeytin Dağı'nda sabahlıyordu.
Tsiku lililonse Yesu amaphunzitsa ku Nyumba ya Mulungu, ndi madzulo ali wonse Iye amachoka kukakhala pa phiri la Olivi usiku wonse.
38 Sabah erkenden bütün halk O'nu tapınakta dinlemek için O'na akın ediyordu.
Ndipo anthu onse amabwera mmamawa kudzamumva Iye ku Nyumba ya Mulungu.

< Luka 21 >