< Від Луки 3 >

1 П’ятнадцятого року царювання Кесаря Тиберія, коли Понтій Пилат правив Юдеєю, Ірод був тетрархом Галілеї, його брат, Филип, був тетрархом земель Трахонії та Ітуреї, а Лісаній був тетрархом Авілінії,
Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
2 коли первосвященниками були Анна та Каяфа, було Слово Боже до Івана, сина Захарії, у пустелі.
Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
3 [Іван] пройшов усю околицю Йордану й проповідував хрещення покаяння для прощення гріхів,
Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
4 як написано в книзі слів пророка Ісаї: «Голос кличе в пустелі: „Приготуйте дорогу Господеві, вирівняйте шляхи для Нього!
Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
5 Нехай кожен яр наповниться і всяка гора та пагорб знизяться. Криві дороги нехай стануть прямими, а нерівні – рівними,
Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
6 і всі люди побачать спасіння Боже“».
Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
7 [Іван] казав так народові, що приходив хреститися в нього: ―Роде гадючий! Хто порадив вам тікати від гніву, що наближається?
Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
8 Чиніть же плоди, достойні покаяння, і не думайте говорити в собі: «Наш батько – Авраам!» Бо кажу вам: Бог може з цього каміння створити дітей для Авраама!
Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
9 Уже й сокира лежить біля коріння дерев! Кожне дерево, яке не приносить доброго плоду, зрубають та вкидають у вогонь.
Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
10 Люди питали його: ―Що ж нам робити?
Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
11 У відповідь він казав: ―Хто має дві сорочки, нехай віддасть одну тому, хто не має жодної, і хто має їжу, хай зробить так само.
Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
12 Прийшли й митники хреститися та спитали його: ―Учителю, а нам що робити?
Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
13 Він відповів: ―Не беріть більше від того, що вам призначено.
Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
14 Воїни теж спитали його: ―А що нам робити? Він відповів: ―Нічого не беріть силою, не обвинувачуйте нікого неправдиво, задовольняйтеся своєю платнею.
Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
15 Народ був в очікуванні, усі розмірковували у своїх серцях про Івана, чи не він Христос.
Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
16 Іван, відповідаючи всім, сказав: ―Я хрещу вас водою, але йде Сильніший за мене, Якому я не достойний розв’язати ремінці Його сандалій. Він буде хрестити вас Духом Святим та вогнем.
Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
17 У Його руці лопата, Він ретельно очистить Свій тік, збиратиме Свою пшеницю до житниці, а полову спалить у невгасимому вогні.
Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
18 І багато іншого казав він, звіщаючи Добру Звістку народу.
Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
19 Але коли він почав осуджувати тетрарха Ірода за Іродіаду, дружину його брата, а також за все зло, що він зробив,
Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
20 то [Ірод] до всього додав ще й те, що замкнув Івана до в’язниці.
Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
21 І сталося, коли хрестився весь народ, і Ісус, охрестившись, молився, розкрилися небеса.
Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
22 І Дух Святий зійшов на Нього в тілесному вигляді, як голуб, і голос із неба пролунав: «Ти Син Мій улюблений, Тебе Я вподобав!»
Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
23 Ісус, починаючи [служіння], був років тридцяти, і всі вважали Його сином Йосифа, сина Іллі,
Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
24 сина Матата, сина Левія, сина Мелхія, сина Янная, сина Йосифа,
mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
25 сина Мататії, сина Амоса, сина Наума, сина Еслі, сина Наггея,
mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
26 сина Маата, сина Мататія, сина Семена, сина Іосиха, сина Йоди,
mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
27 сина Іоана, сина Риса, сина Зоровавеля, сина Салатиїла, сина Нерія,
mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
28 сина Мелхія, сина Аддія, сина Косама, сина Елмадама, сина Іра,
mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
29 сина Ісуса, сина Еліезера, сина Іоріма, сина Матати, сина Левія,
mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
30 сина Симеона, сина Юди, сина Йосифа, сина Йонама, сина Еліакима,
mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
31 сина Мелея, сина Менна, сина Матати, сина Натама, сина Давида,
mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
32 сина Єссея, сина Овіда, сина Воаза, сина Сала, сина Наасона,
mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
33 сина Аммінадава, сина Адміна, сина Арні, сина Есрома, сина Фареса, сина Юди,
mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
34 сина Якова, сина Ісаака, сина Авраама, сина Тара, сина Нахора,
mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
35 сина Серуха, сина Рагава, сина Фалека, сина Евера, сина Селаха,
mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
36 сина Каїнама, сина Арфахада, сина Сима, сина Ноя, сина Ламеха,
mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
37 сина Метусали, сина Еноха, сина Ярета, сина Малелеїла, сина Каїнама,
mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
38 сина Еноса, сина Сета, сина Адама, сина Бога.
mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

< Від Луки 3 >